KUSALA KUDYA (#13445)

Mayamiko akhale kwa Inu, O Ambuye Mulungu wanga! Ndikupemphani Inu mwa Chibvumbulutso chomwechi chimene chasandutsa m’dima kukhala kuwala, kubzolera muchomwechi Kachisi Wanu wobwerezedwa10 bwerezedwa wamangidwa, ndipo Uthenga Wolembedwa waululidwa, ndi Kalata Yolalikidwa yamasulidwa kunditumizira ine ndi iwo amene ali ndi ine chimene chingatithandize kuuluka kunka kumwamba kwa ulemelero Wanu wopambana, ndikutitsuka ife litsilo la kusakhulupilira lomwe lalepheretsa okaika kulowa mu Kachisi wa umodzi Wanu.  
Ine ndine, O Ambuye wanga, amene ndagwira molimba chingwe chachikondi Chanu, ndikukakamirira ku mpindiro wa chisomo ndi chifundo Chanu. Ndikonzereni ine pamodzi ndi okondedwa anga zabwino zadziko lino ndi zadziko limene liri m’kudza. Agawireni iwo, tsono mphatso Zobisika zimene Munawakonzera osankhidwa pakati pazolengedwa Zanu.  
Tsono awa, O Ambuye wanga, ndimasiku amene mwawalamulira a ntchito Anu kusala kudya. Ngodala iye amene asala chakudya chifukwa cha Inu Nokha ndikudzipatula kotheratu kuzinthu zonse koma Inu Nokha. Ndithandizeni ine ndikuwathandiza iwo, O Ambuye wanga, kubvera Inu ndi kusunga malamulo Anu.  
Inu, indetu, Muli ndi mphamvu yochita zomwe Mwasankha. Kulibe Mulungu wina koma Inu Nokha, Wodziwa zonse. Mayamiko onse akhale kwa Mulungu, Ambuye wa maiko onse.

-Bahá'u'lláh
-----------------------

